
The Tower of Babel (Genesis 11: 1-9)
Chicheŵa (Chichewa)
- Tsopano padziko lonse lapansi panali chilankhulo chimodzi ndipo anthu anali kugwiritsa ntchito mawu ofanana.
- Pamene anthuwo analowera chakum'mawa, anapeza chigwa m'dera la Sinara n'kukhazikika kumeneko.
- Kenako anauzana kuti: "Tiyeni tiumbe njerwa tiziotche." Atatero, anayamba kumanga ndi njerwa, n'kumagwiritsa ntchito phula ngati matope omangira.
- Ndiyeno anati: "Tiyeni timange mzinda wathuwathu, ndipo nsanja yake ikafike m'mwamba mwenimweni. Tikatero tidzipangira dzina loti titchuke nalo, ndipo sitibalalikana padziko lonse lapansi."
- Kenako, Yehova anatsikirako kukaona mzinda ndi nsanja imene ana a anthu anali kumanga.
- Pamenepo Yehova anati: "Taonani! Izi n'zimene anthuwa ayamba kuchita popeza ndi amodzi ndipo onse ali ndi chilankhulo chimodzi. Mmene zililimu, angathe kuchita chilichonse chimene akuganiza.
- Choncho, tiyeni tipiteko kuti tikasokoneze chilankhulo chawo, kuti asamamvane polankhula."
- Motero, Yehova anawabalalitsa pamalopo, kuti afalikire padziko lonse lapansi. Zitatero, iwo anasiya pang'onopang'ono kumanga mzindawo.
- Mzindawo unatchedwa Babele, chifukwa kumeneko, Yehova anasokoneza chilankhulo cha anthu onse, ndipo Yehova anabalalitsira anthuwo padziko lonse lapansi.
From: Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Information about Chichewa
Tower of Babel in Bantu languages
Bemba,
Beti,
Chichewa,
Dawida,
Kamba,
Kinyarwanda,
Kirundi,
Kwanyama,
Lingala,
Luba-Katanga,
Luganda,
Luragooli,
Ndebele,
Ndonga,
Northern Sotho,
Sena,
Shona,
Southern Sotho,
Swahili,
Tetela,
Tonga,
Tsonga,
Tswana,
Tumbuka,
Venda,
Xhosa,
Zulu
Other Tower of Babel translations
By language |
By language family
Learn Chinese Characters with the Omniglot Chinese app